Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Amosi 5:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Koma ciweruzo ciyende ngati madzi, ndi cilungamo ngati mtsinje wosefuka.

25. Ngati munabwera nazo kwa Ine nsembe zophera ndi zaufa zaka makumi anai m'cipululu, inu nyumba ya Israyeli?

26. Inde mwasenza hema wa mfumu yanu, ndi tsinde la mafano anu, nyenyezi ya mlungu wanu, amene mudadzipangira.

27. M'mwemo ndidzakutengani kumka nanu kundende kutsogolo kwa Damasiko, ati Yehova, amene dzina lace ndiye Mulungu wa makamu.

Werengani mutu wathunthu Amosi 5