Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Amosi 2:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo ndinakukwezani kucokera m'dziko la Aigupto, ndi kukutsogolerani zaka makumi anai m'cipululu, kuti mulandire dziko la Aamori likhale colowa canu.

11. Ndipo ndinaukitsa mwa ana anu aneneri, ndi mwa anyamata anu Anaziri. Si momwemo, inu ana a Israyeli, ati Yehova?

12. Koma munamwetsa Anaziri vinyo, ndi kulamulira aneneri ndi kuti, Musamanenera.

13. Taonani, ndidzakupsinjani m'malo mwanu, monga lipsinja gareta lodzala ndi mitolo fwa.

14. Ndipo populumukirapo padzasowera waliwiro, ndi wamphamvu; sadzalimbikitsa mphamvu yace, ndi ngwazi siidzapulumutsa moyo wace;

15. ndi wokoka uta sadzalimbika, ndi waliwiro sadzadzipulumutsa; ngakhale woyenda pa akavalo sadzapulumutsa moyo wace;

16. ndi wolimba mtima mwa ngwazi adzathawa wamarisece tsiku lomwelo, ati Yehova.

Werengani mutu wathunthu Amosi 2