Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 6:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Koma Davide ananena ndi Mikala, Ndatero pamaso pa Yehova, amene anandisankha ine ndi kupitirira atate wako ndi banja lace lonse, nandiika ndikhale mtsogoleri wa anthu a Yehova, wa Israyeli, cifukwa cace ndidzasewera pamaso pa Yehova.

22. Ndipo ndidzaonjezanso kukhala ngati munthu woluluka, ndidzakhala wodzicepetsa m'maso a ine mwini; ndipo adzakazi udanenawo, ndi amenewo ndidzalemekezedwa.

23. Ndipo Mikala mwana wamkazi wa Sauli sanaona mwana kufikira tsiku la imfa yace.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 6