Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 5:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo Afilisti anakweranso kaciwiri, natanda m'cigwa ca Refaimu.

23. Ndipo pamene Davide anafunsira kwa Yehova, iye anati, Usamuke, koma ukawazungulire kumbuyo kuti ukawaturukire pandunji pa mkandankhuku.

24. Ndipo kudzali, pakumva iwe kuwayula ku nsonga za mkandankhuku, pomwepo fulumiratu, pakuti pamenepo Yehova waturuka pamaso pako kukakantha khamu la Afilisti.

25. Ndipo Davide anatero, monga Yehova anamlamulira, nakantha Afilisti kuyambira ku Geba kufikira ku Gezeri.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 5