Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 3:34-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Manja anu sanamangidwa, mapazi anu sanalongedwa m'zigologolo;Monga munthu wakugwa ndi anthu oipa momwemo mudagwa inu.Ndipo anthu onse anamliranso.

35. Ndipo anthu onse anadza kudzadyetsa Davide cakudya kukali msana; koma Davide analumbira nati, Mulungu andilange naonjezepo, ngati ndilawa mkate kapena kanthu kena, lisanalowe dzuwa.

36. Ndipo anthu onse anacisamalira, ndipo cinawakomera; ziri zonse adazicita mfumu zidakomera anthu onse.

37. Momwemo anthu onse ndi Aisrayeli onse anazindikira tsiku lija kuti sikunafumira kwa mfumu kupha Abineri mwana wa Neri.

38. Ndipo mfumu inati kwa anyamata ace, Simudziwa kodi kuti kalonga, ndi munthu womveka, wagwa lero m'Israyeli?

39. Ndipo ndikali wofoka ine lero, cinkana ndinadzozedwa mfumu; ndipo amuna awa ana a Zeruya andikakalira mtima; Yehova abwezere wocita coipa monga mwa coipa cace.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 3