Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 3:34-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Manja anu sanamangidwa, mapazi anu sanalongedwa m'zigologolo;Monga munthu wakugwa ndi anthu oipa momwemo mudagwa inu.Ndipo anthu onse anamliranso.

35. Ndipo anthu onse anadza kudzadyetsa Davide cakudya kukali msana; koma Davide analumbira nati, Mulungu andilange naonjezepo, ngati ndilawa mkate kapena kanthu kena, lisanalowe dzuwa.

36. Ndipo anthu onse anacisamalira, ndipo cinawakomera; ziri zonse adazicita mfumu zidakomera anthu onse.

37. Momwemo anthu onse ndi Aisrayeli onse anazindikira tsiku lija kuti sikunafumira kwa mfumu kupha Abineri mwana wa Neri.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 3