Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 23:23-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Iye ndiye waulemu koposa makumi atatuwo, koma sadafikana ndi atatu oyamba. Ndipo Davide anamuika kuyang'anira olindirira ace.

24. Asaheli mbale wa Yoabu anali wa makumi atatuwo; Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu;

25. Sama Mharodi, Elika Mharodi;

26. Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi Mtekoi.

27. Abiyezeri M-anetori, Mebunai Mhusati;

28. Zalimoni M-ahohi, Maharai Mnefati;

29. Helebi mwana wa Baana Mnetofati, ltai mwana wa Ribai wa ku Gibeya wa ana a Benjamini;

30. Benaya Mpiratoni, Hidai wa ku timitsinje ta Gaasi;

31. Abialiboni M-aribati, Azmaveti Mbahurimi;

32. Eliaba Mshaliboni wa ana a Jaseni, Jonatani;

33. Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari;

34. Elifaleti mwana wa Ahasibai, mwana wa Mmaacha, Eliamu mwana wa Ahitofeli Mgiloni;

35. Hezra wa ku Karimeli, Paarai M-aribi;

36. Igali mwana wa Natani wa ku Zoba, Bani Mgadi;

37. Zeleki M-amoni, Naharai Mbeeroti, onyamula zida za Yoabu mwana wa Zeruya;

38. Ira M-itri, Garebi M-itri;

39. Uriya Mhiti; onse pamodzi anali makumi atatu mphambu asanu ndi awiri.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 23