23. Iye ndiye waulemu koposa makumi atatuwo, koma sadafikana ndi atatu oyamba. Ndipo Davide anamuika kuyang'anira olindirira ace.
24. Asaheli mbale wa Yoabu anali wa makumi atatuwo; Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu;
25. Sama Mharodi, Elika Mharodi;
26. Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi Mtekoi.
27. Abiyezeri M-anetori, Mebunai Mhusati;
28. Zalimoni M-ahohi, Maharai Mnefati;
29. Helebi mwana wa Baana Mnetofati, ltai mwana wa Ribai wa ku Gibeya wa ana a Benjamini;
30. Benaya Mpiratoni, Hidai wa ku timitsinje ta Gaasi;
31. Abialiboni M-aribati, Azmaveti Mbahurimi;