Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 18:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Munthuyo nanena ndi Yoabu, Ndingakhale ndikalandira ndarama cikwi m'dzanja langa, koma sindikadasamula dzanja langa pa mwana wa mfumu; pakuti m'kumva kwathu mfumu inalamulira inu ndi Abisai ndi ltai, kuti, Cenjerani munthu yense asakhudze mnyamatayo Abisalomu.

13. Ndikadacita conyenga pa moyo wace, palibe mrandu ubisika kwa mfumu; ndipo inu nomwe mukadanditsuta.

14. Pomwepo Yoabu anati, Sindiyenera kucedwa nawe. Natenga mikondo itatu nagwaza nayo mtima wa Abisalomu alikukhala wamoyo pakati pa mtengowo.

15. Ndipo anyamata khumi onyamula zida zace za Yoabu anamzungulira Abisalomu namkantha namupha.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 18