Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 14:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Yoabu anatumiza ku Tekowa, natenga kumeneko mkazi wanzeru, nanena naye, Ukokomezeke monga mfedwa, nubvale zobvala za pamaliro, osadzola mafuta, koma ukhale ngati munthu wamkazi wakulira akufa nthawi yaikuru.

3. Nulowe kwa mfumu, nulankhule nayo monga momwemo. Comweco Yoabu anampangira mau.

4. Ndipo pamene mkazi wa ku Tekowayo anati alankhule ndi mfumuyo, anagwa nkhope yace pansi namlambira, nati, Ndithandizeni mfumu.

5. Ndipo mfumuyo inanena naye, Usowanji? iye nayankha, Zoonadi ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga ana mwalira.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 14