Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 13:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo Davide anatumiza mau kwao kwa Tamara, kuti, Upite ku nyumba ya mlongo wako Amnoni, numkonzere cakudya,

8. Comweco Tamara anapita ku nyumba ya mlongo wace Amnoni; ndipo iye anali cigonere. Ndipo anatenga ufa naukanda naumba timitanda pamaso pace, nakazinga timitandato.

9. Ndipo anatenga ciwaya natiturutsa pamaso pace; koma anakana kudya. Ndipo Amnoni anati, Anthu onse aturuke kundisiya ine. Naturuka onse, kumsiya.

10. Ndipo Amnoni anati kwa Tamara, Bwera naco cakudya kucipinda kuti ndikadye ca m'manja mwako. Ndipo Tamara anatenga timitanda anatipangato, nabwera nato kucipinda kwa Amnoni mlongo wace.

11. Ndipo pamene anabwera nato pafupi kuti adye, iye anamgwira, nanena naye, Idza nugone nane, mlongo wanga.

12. Koma iye anamyankha nati, lai, mlongo wanga, usandicepetsa ine, pakuti cinthu cotere siciyenera kucitika m'Israyeli, usacita kupusa kumeneku.

13. Ndipo ine, manyazi anga ndidzapita nao kuti? ndipo iwenso udzakhala ngati wina wa zitsiru m'Israyeli. Cifukwa cace tsono ulankhule ndi mfumu; iyeyu sadzakukaniza ine.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 13