Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 12:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo kwa wolemerayo kunafika mlendo, ndipo iye analeka kutengako mwa zoweta zace zazing'ono ndi zazikuru, kuphikira mlendo amene anafika kwa iye, koma anatenga mwana wa nkhosa wa wosaukayo, naphikira munthu amene anafika kwa iye.

5. Pamenepo mkwiyo wa Davide unayaka ndithu pa munthuyo, nati kwa Natani, Pali Yehova, munthu amene anacita ici, ayenera kumupha;

6. ndipo adzabwezera mwa mwana wa nkhosayo ena anai, cifukwa anacita ici osakhala naco cifundo.

7. Ndipo Natani ananena kwa Davide, Munthuyo ndi inu nomwe. Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, Ndinakudzoza ukhale mfumu ya Israyeli, ndinakupulumutsa m'dzanja la Sauli;

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 12