Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 12:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Ndipo anafika kwa iye nanena naye, Pa mudzi wina panali anthu awiri; wina wolemera, wina wosauka.

2. Wolemerayo anali nazo zoweta zazing'ono ndi zazikuru zambiri ndithu;

3. koma wosaukayo analibe kanthu kena koma kamwana kakakazi ka nkhosa, kamene anakagula ndi kukaweta; ndipo kameneko kanakula naye pamodzi ndi ana ace. Kanadyako cakudya cace ca iye yekha, kanamwera m'cikho ca iye yekha, kanagona pa cifukato cace, ndipo kanali kwa iye ngati mwana wace wamkazi.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 12