Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 9:22-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Mamwemo mfumu Solomo inaposa mafumu onse a pa dziko lapansi, kunena za cuma ndi nzeru.

23. Ndipo mafumu onse a pa dziko lapansi anafuna nkhope ya Solomo, kudzamva nzeru zace Mulungu adazilonga m'mtima mwace.

24. Nabwera nao munthu yense mtulo wace, zipangizo zasiliva, ndi zipangizo zagolidi, zobvala, ndi zobvala za nkhondo, ndi zonunkhira, akavalo, ndi nyuru; momwemo caka ndi caka.

25. Ndipo Solomo anali nazo zipinda zikwi zinai za akavalo ndi magareta, ndi apakavalo zikwi khumi ndi ziwiri; nawaika m'toidzi ya magareta, ndi m'Yerusalemu kwa mfumu.

26. Ndipo analamulira mafumu onse kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti, ndi ku malire a ku Aigupto.

27. Ndipo mfumu inacurukitsa siliva m'Yerusalemu ngati miyala; ndi mikungudza anailinganiza ndi mikuyu iri kumadambo kucuruka kwace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 9