Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 8:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, zitatha zaka makumi awiri m'mene anamanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba yace yace,

2. Solomo anamanga midzi imene Huramu adampatsa, nakhalitsamo ana a Israyeli.

3. Ndipo Solomo anamuka ku Hamati Zoba, naugonjetsa.

4. Ndipo anamanga Tadimori m'cipululu, ndi midzi yonse yosungiramo cuma, imene anaimanga m'Hamati.

5. Anamanganso Betihoroni wa kumtunda, ndi Betihoroni wa kunsi, midzi ya malinga yokhala nao malinga, zitseko, ndi mipiringidzo;

6. ndi Balati, ndi midzi yonse yosungiramo cuma anali nayo Solomo, ndi midzi yonse ya magareta ace, ndi midzi ya apakavalo ace, ndi zonse anazifuna Solomo kuzimanga zomkondweretsa m'Yerusalemu, ndi m'Lebano, ndi m'dziko lonse la ufumu wace.

7. Ndipo anthu onse otsala mwa Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, osati Aisrayeli,

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 8