Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 7:21-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndi munthu yense wakupita pa nyumba iyi yaitali adzadabwa nayo, nadzati, Yeliova ana tero ndi dziko lino ndi nyumba yino cifukwa ninji?

22. Ndipo adzayankha, Popeza anasiya Yehova Mulungu wa makolo ao amene anawaturutsa m'dziko la Aigupto, nagwira milungu yina, nailambira ndi kuitumikira; cifukwa cace anawagwetsera coipa ici conse.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 7