Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 36:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo pofikanso nyengo, mfumu Nebukadinezara anatumiza anthu abwere naye ku Babulo, pamodzi ndi zipangizo zokoma za nyumba ya Yehova; nalonga Zedekiya mbale wace mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.

11. Zedekiya anali wa zaka makumi awiri mphambu cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi ndi cimodzi,

12. nacita coipa pamaso pa Yehova Mulungu wace; sanadzicepetsa kwa Yeremiya mneneri wakunena zocokera pakamwa pa Yehova.

13. Ndiponso anapandukana naye mfumu Nebukadinezara, amene adamlumbiritsa pa Mulungu; koma anaumitsa khosi lace, nalimbitsa mtima wace kusatembenukira kwa Yehova Mulungu wa Israyeli,

14. Ndiponso ansembe akulu onse ndi anthu anacurukitsa zolakwa zao, monga mwa zonyansa zonse za amitundu, nadetsa nyumba ya Yehova, imene ana patula m'Yerusalemu.

15. Ndipo Yehova Mulungu wa makolo ao anatumiza kwa iwo, ndi dzanja la mithenga yace, nalawirira mamawa kuituma, cifukwa anamvera cifundo anthu ace, ndi pokhala pace;

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 36