Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 32:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitatha zinthu izi zokhulupirika, anadza Sanakeribu mfumu ya Asuri, nalowera Yuda, namangira midzi yamalinga misasa, nati adzigonjetsere iyi.

2. Ndipo pakuona Hezekiya kuti wadza Sanakeribu, ndi kuti nkhope yace inalunjikitsa kuyambana nkhondo ndi Yerusalemu,

3. anapangana ndi akuru ace ndi amphamvu ace, kutseka madzi a m'akasupe okhala kunja kwa mudzi; namthandiza iwo.

4. Nasonkhana anthu ambiri, natseka akasupe onse, ndi mtsinje woyenda pakati pa dziko, ndi kuti, Angafike mafumu a Asuri ndi kupeza madzi ambiri.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 32