Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 28:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. nanena nao, Musalowa nao andende kuno; pakuti inu mukuti mutiparamulitse kwa Yehova, kuonjezera pa macimo athu ndi zoparamula zathu; pakuti taparamula kwakukuru, ndipo pali mkwiyo waukali pa Israyeli.

14. Pamenepo eni zida anasiya andende ndi zofunkha pamaso pa akalonga ndi msonkhano wonse.

15. Nanyamuka amuna ochulidwa maina, natenga andende, nabveka ausiwa onse mwa iwo ndi zofunkhazo, nawapatsa zobvala, ndi nsapato, nawadyetsa ndi kuwamwetsa, nawadzoza, nasenza ofoka ao onse pa aburu, nafika nao ku Yeriko, mudzi wa migwalangwa, kwa abale ao; nabwerera iwo kunka ku Samariya.

16. Nthawi yomweyi mfumu Ahazi anatumiza kwa mafumu a Asuri amthandize.

17. Pakuti Aedomu anadzanso, nakantha Yuda, natenga andende.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 28