Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 26:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Uziya anali wa zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi asanu mphambu ziwiri; ndi dzina la mace ndiye Yekoliya wa ku Yerusalemu.

4. Nacita iye zoongoka pamaso pa Yehova, monga mwa zonse adazicita atate wace Amaziya.

5. Ndipo iye anali munthu wakufuna Mulungu masiku a Zekariya, ndiye wozindikira masomphenya a Mulungu; ndipo masiku akufunira Yehova iye, Mulungu anamlemereza;

6. popeza anaturuka, nayambana ndi Afilisti, nagamula linga la Gati, ndi linga la Yabine, ndi linga la Asidodi; namanga midzi m'dziko la Asidodi, ndi mwa Afilisti.

7. Ndipo Mulungu anamthandiza poyambana ndi Afilisti, ndi Aarabu okhala m'Guribaala, ndi Ameuni.

8. Ndipo Aamoni anampatsa Uziya mitulo; ndi dzina lace linabuka mpaka polowera ku Aigupto; pakuti analil mbika cilimbikire.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 26