Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 24:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yoasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi anai; ndi dzina la mace ndiye Zibiya wa ku Beereseba.

2. Ndipo Yoasi anacita zoongoka pamaso pa Yehova masiku onse a Yehoyada wansembe.

3. Ndipo Yehoyada anamtengera akazi awiri, nabala ana amuna ndi akazi.

4. Ndipo pambuyo pace mumtima mwa Yoasi munali cofuna kukonzanso nyumba ya Yehova.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 24