Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 21:13-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. koma mwayenda m'njira ya mafumu a Israyeli, ndi kucititsa Yuda ndi okhala m'Yerusalemu cigololo, monga umo anacitira cigololo a nyumba ya Ahabu, mwaphanso abale anu a nyumba ya atate wanu, ndiwo abwino akuposa inu;

14. taonani, Yehova adzakantha anthu anu, ndi ana anu, ndi akazi anu, ndi cuma canu conse, makanthidwe akuru;

15. ndipo mudzadwala kwakukuru nthenda yamatumbo, mpaka matumbo anu adzaturuka cifukwa ca nthendayi tsiku ndi tsiku.

16. Ndipo Yehova anautsira Yehoramu mzimu wa Afilisti, ndi wa Aarabu okhala pambali pa Akusi;

17. ndiwo anakwerera Yuda, nathyolamo, nalanda cuma conse cinapezeka m'nyumba ya mfumu, ndi ana ace omwe, ndi akazi ace, osamsiyira mwana, koma Yehoahazi yekha mwana wace wamng'ono.

18. Ndi pambuyo pace pa izi zonse Yehova anamdwalitsa m'matumbo ace ndi nthenda yosacira nayo.

19. Ndipo kunali, itapita nthawi, pakutha pace pa zaka ziwiri, anaturuka matumbo ace mwa nthenda yace namwalira nazo nthenda zoipa, Ndipo anthu ace sanampserezera zonunkhira, monga umo anapserezera makolo ace.

20. Anali wa zaka makumi atatu mphambu ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu, namuka wopanda wina womlakalaka; ndipo anamuika m'mudzi wa Davide, koma si m'manda a mafumu ai.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 21