Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 18:26-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. nimuziti, Itero mfumu, Mumuike uyu m'kaidi, ndi kumdyetsa cakudya comsautsa, ndi kummwetsa madzi omsautsa, mpaka ndikabwera mumtendere.

27. Nati Mikaya, Mukakabwera ndi mtendere konse, Yehova sananena mwa ine. Natiiye, Tamverani, anthu inu nonsenu.

28. Momwemo mfumu ya Israyeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakwera kumka ku Ramoti Gileadi.

29. Ndi mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Ndidzadzizimbaitsa ndi kulowa kunkhondo, koma inu bvalani zobvala zanu. Nidzizimbaitsa mfumu ya Israyeli, namuka iwo kunkhondo.

30. Mfumu ya Aramu tsono idauza akapitao a magareta ace, ndi kuti, Musayambana ndi ang'ono kapena akuru, koma ndi mfumu ya Israyeli yekha.

31. Ndipo kunali, pamene akapitao a magareta anaona Yehosafati, anati, Ndiye mfumu ya Israyeli. Potero anamtembenukira kuyambana naye; koma Yehosafati anapfuula, namthandiza Yehova; ndipo Mulungu anawapambukitsa amleke.

32. Ndipo kunali, pamene akapitao a magareta anaona kuti sanali mfumu ya Israyeli anabwerera osamtsatanso.

33. Ndipo munthu anaponya mubvi wace ciponyeponye, namlasa pakati pa maluma a maraya ace acitsulo. Potero anati kwa woyendetsa garetayo, Tembenuza dzanja lako, nundicotse ku khamu la nkhondo kuno, pakuti ndalasidwa.

34. Ndipo nkhondo inakula tsiku lija; koma mfumu ya Israyeli inagwirizizil ka m'gareta wace popenyana ndi Aaramu mpaka madzulo, namwalira nthawi yakulowa dzuwa.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 18