Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 18:24-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Nati Mikaya, Tapenya, udzaona tsiku lolowa iwe m'cipinda cam'kati kubisala.

25. Ndipo mfumu ya Israyeli inati, Mumtenge Mikaya, mukambweze kwa Amoni kazembe wa mudzi, ndi kwa Yoasi mwana wa mfumu;

26. nimuziti, Itero mfumu, Mumuike uyu m'kaidi, ndi kumdyetsa cakudya comsautsa, ndi kummwetsa madzi omsautsa, mpaka ndikabwera mumtendere.

27. Nati Mikaya, Mukakabwera ndi mtendere konse, Yehova sananena mwa ine. Natiiye, Tamverani, anthu inu nonsenu.

28. Momwemo mfumu ya Israyeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakwera kumka ku Ramoti Gileadi.

29. Ndi mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Ndidzadzizimbaitsa ndi kulowa kunkhondo, koma inu bvalani zobvala zanu. Nidzizimbaitsa mfumu ya Israyeli, namuka iwo kunkhondo.

30. Mfumu ya Aramu tsono idauza akapitao a magareta ace, ndi kuti, Musayambana ndi ang'ono kapena akuru, koma ndi mfumu ya Israyeli yekha.

31. Ndipo kunali, pamene akapitao a magareta anaona Yehosafati, anati, Ndiye mfumu ya Israyeli. Potero anamtembenukira kuyambana naye; koma Yehosafati anapfuula, namthandiza Yehova; ndipo Mulungu anawapambukitsa amleke.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 18