Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 18:18-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Nati iye, Cifukwa cace tamvani mau a Yehova, Ndinaona Yehova alikukhala pa mpando wace wacifumu, ndi khamu lonse lakumwamba lirikuima pa dzanja lace lamanja, ndi pa dzanja lace lamanzere.

19. Nati Yehova, Adzamnyenga Ahabu mfumu ya Israyeli ndani, kuti akwereko, nagwe ku Ramoti Gileadi? Nati wina mwakuti, wina mwakuti.

20. Ndipo unaturuka mzimu, nuima pamaso pa Yehova, nuti, Ndidzamnyenga ndine. Ndipo Yehova, ananena nao, Ndi ciani?

21. Nuti uwu, Ndidzaturuka ndi kukhala mzimu wonama m'kamwa mwa aneneri ace onse. Nati Iye, Udzamnyengadi, nudzakhoza; turuka, ukatero kumene.

22. Ndipo tsono taonani, Yehova analonga mzimu wabodza m'kamwa mwa aneneri anu awa, nakunenetserani coipa Yehova.

23. Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenana anayandikira, nampanda Mikaya patsaya, nati, Mzimu wa Yehova wandicokera bwanji kulankhula ndi iwe?

24. Nati Mikaya, Tapenya, udzaona tsiku lolowa iwe m'cipinda cam'kati kubisala.

25. Ndipo mfumu ya Israyeli inati, Mumtenge Mikaya, mukambweze kwa Amoni kazembe wa mudzi, ndi kwa Yoasi mwana wa mfumu;

26. nimuziti, Itero mfumu, Mumuike uyu m'kaidi, ndi kumdyetsa cakudya comsautsa, ndi kummwetsa madzi omsautsa, mpaka ndikabwera mumtendere.

27. Nati Mikaya, Mukakabwera ndi mtendere konse, Yehova sananena mwa ine. Natiiye, Tamverani, anthu inu nonsenu.

28. Momwemo mfumu ya Israyeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakwera kumka ku Ramoti Gileadi.

29. Ndi mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Ndidzadzizimbaitsa ndi kulowa kunkhondo, koma inu bvalani zobvala zanu. Nidzizimbaitsa mfumu ya Israyeli, namuka iwo kunkhondo.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 18