Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 15:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo Yuda yense anakondwera nalo lumbirolo; pakuti adalumbira ndi mtima wao wonse, namfunafuna ndi cifuno cao conse; ndipo anampeza; ndi Yehova anawapumulitsa pozungulirapo.

16. Maaka yemwe, mai wace wa Asa, mfumu, anamcotsa uyu asakhalenso mai wa ufumu, popeza anapanga fano loopsa la Asera; ndipo Asa analikha fano lace, naliphwanyaphwanya, nalitenthera ku mtsinje wa Kedroni.

17. Cinkana misanje siinacotsedwa m'Israyeli, mtima wa Asa unali wangwiro masiku ace onse.

18. Ndipo analowa nazo zopatulika za atate wace, ndi zopatulika zace zace, ku nyumba ya Mulungu; ndizo siliva, ndi golidi, ndi zipangizo.

19. Ndipo panalibenso nkhondo mpaka Asa atakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zinai.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 15