17. Ndipo Abiya ndi anthu ace anawakantha makanthidwe akuru; nagwa, nafa amuna osankhika zikwi mazanaasanu a Israyeli.
18. Momwemo anacepetsedwa ana a Israyeli nthawi ija, nalakika ana a Yuda; popeza anatama Yehova Mulungu wa makolo ao.
19. Ndipo Abiya analondola Yerobiamu, namlanda midzi yace, Beteli ndi miraga yace, ndi Yesana ndi miraga yace, ndi Efroni ndi miraga yace.