Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 13:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo caka cakhumi mphambu zisanu ndi zitatu ca Yerobiamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda.

2. Anakhala mfumu m'Yerusalemu zaka zitatu; ndi dzina la mace ndiye Mikaya mwana wamkazi wa Uriyeli wa ku Gibeya. Ndipo panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yerobiamu.

3. Ndipo Abiya anayambana nkhondo ali ndi khamu la ngwazi za nkhondo, amuna osankhika zikwi mazana anai; Yerobiamu atandandalitsa nkhondo yace ilimbane naye ndi amuna osankhika zikwi mazana asanu ndi atatu, ndiwo ngwazi zamphamvu.

4. Ndipo Abiya anaimirira pa phiri la Zemaraimu, ndilo ku mapiri a Efraimu, nati, Mundimvere Yerobiamu ndi Aisrayeli onse;

5. simudziwa kodi kuti Yehova Mulungu wa Israyeli anapereka ciperekere ufumu wa Israyeli kwa Davide, kwa iye ndi ana ace, ndi pangano la mcere?

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 13