Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 9:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndi mlonda anafotokozera, kuti, Wawafika, koma wosabwera; ndipo kuyendetsako kukunga kuyendetsa kwa Yehu mwana wa Nimsi, pakuti ayendetsa moyaruka.

21. Nati Yoramu, Manga. Namanga gareta wace, Ndipo Yoramu mfumu ya Israyeli ndi Ahaziya mfumu ya Yuda anaturuka yense m'gareta wace, naturuka kukakomana ndi Yehu, nakomana naye pa munda wa Naboti m'Yezreeli.

22. Ndipo kunali, pamene Yoramu anaona Yehu, anari, Mtendere kodi, Yehu? Nati iye, Ngwanji mtendere pokhala cacuruka cigololo ndi nyanga zace za mai wako Yezebeli?

23. Natembenuza Yoramu manja ace, nathawa, nati kwa Ahaziya, Ciwembu, Ahaziya.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 9