Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 8:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo caka cacisanu ca Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israyeli, pokhala Yehosafati mfumu ya Yuda, Yehoramu mwana wa Yehosafati analowa ufumu.

17. Ndiye wa zaka makumi atatu ndi ciwiri polowa ufumu wace, nacita ufumu zaka zisanu ndi zitatu ku Yerusalemu.

18. Nayenda m'njira ya mafumu a Israyeli, m'mene inacitira nyumba ya Ahabu; pakuti mkazi wace ndiye mwana wa Ahabu, nacita iye coipa pamaso pa Yehova.

19. Koma Yehova sanafuna kuononga Yuda, cifukwa ca Davide mtumiki wace monga adamuuza, kuti adzampatsa nyali ya kwa ana ace kosalekeza.

20. Masiku ace Aedomu anapanduka ku ulamuliro wa Yuda, nadziikira mfumu okha.

21. Pamenepo Yoramu anaoloka kumka ku Zairi, ndi magareta ace onse pamodzi naye; nauka iye usiku, nakantha Aedomu akumzinga ndi nduna za magareta, nathawira anthu ku mahema ao.

22. Motero Aedomu anapanduka ku ulamuliro wa Yuda mpaka lero lino. Ndipo Alibina anapanduka nthawi yomweyi.

23. Ndi macitidwe ena a Yoramu, ndi zonse anazicita, sizinalembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 8