Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 24:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Zedekiya anali wa zaka makumi awiri mphambu cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi ndi cimodzi m'Yerusalemu; ndi dzina la mace ndiye Hamutala mwana wa Yeremiya wa ku Libina.

19. Nacita iye coipa pamaso pa Yehova, monga mwa zonse adacita Yoyakimu.

20. Pakuti mwa mkwiyo wa Yehova zonse zidacitika m'Yerusalemu ndi m'Yuda, mpaka adawataya pamaso pace; ndipo Zedekiya anapandukira mfumu ya Babulo.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 24