Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 21:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Nayenda iye m'njira monse anayendamo atate wace, natumikira mafano anawatumikira atate wace, nawagwadira;

22. nasiya Yehova Mulungu wa makolo ace, sanayenda m'njira ya Yehova.

23. Ndipo anyamata ace a Amoni anamcitira ciwembu, napha mfumuyo m'nyumba yace yace.

24. Koma anthu a m'dzikomo anapha onse akumcitira ciwembu mfumu Amoni; ndipo anthu a m'dzikomo anamlonga ufumu Yosiya mwana wace m'malo mwace.

25. Macitidwe ena tsono a Amoni adawacita, salembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

26. Naikidwa iye m'manda mwace m'munda wa Uza; nakhalamfumum'malo mwace Yosiya mwana wace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 21