Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 19:33-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Adzabwerera njira yomweyo anadzera, ndipo sadzalowa m'mudzi muno, ati Yehova.

34. Pakuti ndidzacinjiriza mudzi uno kuupulumutsa, cifukwa ca Ine mwini, ndi cifukwa ca Davide mtumiki wanga.

35. Ndipo kunali, usiku womwewo mthenga wa Yehova anaturuka, nakantha m'misasa ya Aasuri zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu, ndipo pouka anthu mamawa, taonani, onsewo ndi mitembo.

36. Nacoka Sanakeribu mfumu ya Asuri, namuka, nabwerera, nakhala ku Nineve.

37. Ndipokunali popembedza iye m'nyumba ya Nisiroki mulungu wace, Adrameleki ndi Sarezere anamkantha ndi lupanga; napulumukira ku dziko la Ararati. Ndipo Esarihadoni mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 19