Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 16:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka cakhumi mphambu zisanu ndi ziwiri ca Peka mwana wa Remaliya Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.

2. Ahazi anali wa zaka makumi awiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi m'Yerusalemu; koma sanacita zoongoka pamaso pa Yehova Mulungu wace, ngati Davide kholo lace;

3. popeza anayenda m'njira ya mafumu a Israyeli, napititsanso mwana wace pamoto, monga mwa zonyansa za amitundu amene Yehova anawaingitsa pamaso pa ana a Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 16