Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 12:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka cacisanu ndi ciwiri ca Yehu, Yoasi analowa ufumu wace; nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi anai; ndi dzina la mai wace ndiye Zibiya wa ku Beereseba.

2. Ndipo Yoasi anacita zoongoka pamaso pa Yehova masiku ace onse, m'mene anamlangizira wansembe Yehoyada.

3. Koma misanje sanaicotsa; anthu anapherabe nsembe, nafukiza komisanje.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 12