Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 8:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pamene Samueli anakalamba, anaika ana ace amuna akhale oweruza a Israyeli.

2. Dzina la mwana wace woyamba ndiye Yoeli, ndi dzina la waciwiri ndiye Abiya; ndiwo oweruza a ku Beereseba.

3. Ndipo ana ace sanatsanza makhalidwe ace, koma anapambukira ku cisiriro, nalandira cokometsera mlandu, naipitsa kuweruza.

4. Pamenepo akuru onse a Israyeli anasonkhana, nadza kwa Samueli ku Rama;

5. nanena naye, Taonani, mwakalamba, ndipo ana anu satsanza makhalidwe anu; tsono, mutilongere mfumu kuti ikatiweruze, monga umo mucitidwa m'mitundu yonse ya anthu.

6. Koma cimeneci sicinakondweretsa Samueli, pamene iwo anati, Tipatseni mfumu kuti itiweruze. Ndipo Samueli anapemphera kwa Yehova.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 8