Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 25:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo tsono ndamva kuti muli nao osenga nkhosa; abusa anu amene anali ndi ife, sitinawacititsa manyazi, ndipo panalibe kanthu kao kadasowa, nthawi yonse anakhala iwo ku Karimeli.

8. Mufunse anyamata anu, adzakuuzani; cifukwa cace muwakomere mtima anyamata awa, pakuti tirikufika tsiku labwino; mupatse ciri conse muli naco m'dzanja lanu, kwa anyamata anu, ndi kwa mwana wanu Davide.

9. Ndipo pakufika anyamata a Davide, analankhula ndi Nabala monga mau aja onse m'dzina la Davide, naleka.

10. Koma Nabala anayankha anyamata a Davide nati, Davide ndani? ndi mwana walese ndani? Makono ano pali anyamata ambiri akungotaya ambuye ao.

11. Kodi ndidzatenga mkate wanga, ndi madzi anga, ndi nyama imene ndinaphera osenga nkhosa anga, ndi kuzipatsa anthu amene sindidziwa kumene afumira?

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 25