Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 24:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo unatsimikiza lero lino kuti wandicitira zabwino cifukwa sunandipha pamene Yehova anandipereka m'dzanja lako.

19. Pakuti munthu akapeza mdani wace, adzamleka kodi kuti acoke bwino? Cifukwa cace Yehova akubwezere zabwino pa ici unandicitira ine lero lomwe.

20. Ndipo tsono taona ndidziwa kuti udzakhala mfumu ndithu, ndi kuti ufumu wa Israyeli udzakhazikika m'dzanja lako.

21. Cifukwa cace tsono undilumbirire ndi Yehova, kuti sudzatha mbeu yanga nditamuka ine, ndi kuti sudzaononga dzina langa m'nyumba ya atate wanga.

22. Ndipo Davide analumbirira Sauli. Sauli namuka kwao; koma Davide ndi anthu ace anakwera kumka kungaka.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 24