Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 22:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo mmodzi wa ana a Ahimeleki, mwana wa Ahitubu, dzina lace ndiye Abyatara, anapulumuka, nathawira kwa Davide.

21. Ndipo Abyatara anadziwitsa Davide kuti Sauli anapha ansembe a Yehova.

22. Ndipo Davide anati kwa Abyatara, Tsiku lija Doegi wa ku Edomu anali kumeneko, ndinadziwiratu kuti adzauzadi Sauli; ine ndinafetsa anthu onse a nyumba ya atate wako.

23. Ukhale ndi ine, usaopa; popeza iye wakufuna moyo wanga afuna moyo wako; koma ndi ine udzakhala mosungika.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 22