Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 22:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pamenepo mfumu inati kwa Doegi, Potoloka iwe nuwaphe ansembewo. Ndipo Doegi wa ku Edomu anapotoloka, nagwera ansembewo, napha tsikulo makumi asanu ndi atatu mphambu asanu akubvala efodi wabafuta.

19. Ndipo anakantha Nobi ndiwo mudzi wa ansembe ndi lupanga lakuthwa, anthu amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ng'ombe ndi aburu, ndi nkhosa, ndi lupanga lakuthwa.

20. Ndipo mmodzi wa ana a Ahimeleki, mwana wa Ahitubu, dzina lace ndiye Abyatara, anapulumuka, nathawira kwa Davide.

21. Ndipo Abyatara anadziwitsa Davide kuti Sauli anapha ansembe a Yehova.

22. Ndipo Davide anati kwa Abyatara, Tsiku lija Doegi wa ku Edomu anali kumeneko, ndinadziwiratu kuti adzauzadi Sauli; ine ndinafetsa anthu onse a nyumba ya atate wako.

23. Ukhale ndi ine, usaopa; popeza iye wakufuna moyo wanga afuna moyo wako; koma ndi ine udzakhala mosungika.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 22