Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 14:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo Sauli ndi anthu onse amene anali naye anaunjikana pamodzi, naturukira kunkhondoko; ndipo taonani, munthu yense anakantha mnzace ndi lupanga, ndipo panali kusokonezeka kwakukuru.

21. Ndiponso Ahebri akukhala nao Afilisti kale, amene anaturuka m'dziko lozungulira kukaiowa nao kuzithando; iwonso anatembenukira kuti akakhale ndi Aisrayeli amene anali ndi Sauli ndi Jonatani.

22. Anateronso Aisrayeli onse akubisala m'phiri la Efraimu, pakumva kuti Afilisti anathawa, iwo anawapitikitsa kolimba kunkhondoko.

23. Comweco Yehova anapulumutsa Israyeli tsiku lija; ndipo nkhondo inapitirira pa Betaveni.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 14