Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 12:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndikalipo ine; citani umboni wonditsutsa pamaso pa Yehova, ndi pamaso pa wodzozedwa wace; ndinalanda ng'ombe ya yani? kapena ndinalanda buru wa yani? ndinanyenga yani? ndinasautsa yani? ndinalandira m'manja mwa yani cokometsera mlandu kutseka naco maso anga? ngati ndinatero ndidzacibwezera kwa inu.

4. Ndipo iwo anati, Simunatinyenga, kapena kutisautsa, kapena kulandira kanthu m'manja mwa wina ali yense.

5. Ndipo iye ananena nao, Yehova ali mboni yanu, ndi wodzozedwa wace ali mboni lero kuti simunapeza kanthu m'dzanja langa, Nati iwo, iye ali mboni.

6. Ndipo Samueli ananena ndi anthuwo, Yehova ndiye amene anaika Mose ndi Aroni, naturutsanso makolo anu m'dziko la Aigupto,

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 12