Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 12:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pakuti Yehova sadzasiya anthu ace cifukwa ca dzina lace lalikuru; pakuti kudamkomera Yehova kukuyesani inu anthu a iye yekha.

23. Ndipo inenso, kukhale kutali ndi ine, kucimwira Yehova ndi kuleka kukupemphererani; koma ndidzakulangizani njira yabwino ndi yolungama.

24. Koma mumuope Yehova, ndi kumtumikira koona, ndi mtima wanu wonse; lingalirani zinthu zazikuruzo iye anakucitirani.

25. Koma mukaumirirabe kucita coipa, mudzaonongeka, inu ndi mfumu yanu yomwe.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 12