Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 5:6-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Beera mwana wace, amene Tigilati Pilesere wa ku Asuri anamtenga ndende; ndiye kalonga wa Arubeni.

7. Ndi abale ace monga mwa mabanja ao, powerenga cibadwidwe ca mibadwo yao: akuru ndiwo Yeyeli, ndi Zekariya,

8. ndi Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoeli, wokhala ku Aroeri, ndi kufikira ku Nebo ndi Baala-meoni;

9. ndi kum'mawa anakhala mpaka polowera kucipululu kuyambira mtsinje wa Firate; pakuti zoweta zao zinacuruka m'dziko la Gileadi.

10. Ndipo masiku a Sauli anagwirana nkhondo ndi Ahagiri, amene adagwa ndi dzanja lao; ndipo anakhala m'mahema mwao kum'mawa konse kwa Gileadi.

11. Ndi ana a Gadi anakhala pandunji pao m'dziko la Basana mpaka Saleka:

12. Yoeli mkuru wao, ndi Safamu waciwiri, ndi Yanai, ndi Safati m'Basana;

13. ndi abale ao a; nyumba za makolo ao: Mikaeli, ndi Mesulamu, ndi Seba, ndi Yorai, ndi Yakani, ndi Ziya, ndi Eberi; asanu ndi awiri.

14. Awa ndi ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Gileadi, mwana wa Mikaeli, mwana wa Yesisai, mwana wa Yado, mwana wa Buzi,

15. Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, ndiye mkulu wa nyumba za makolo ao.

16. Ndipo anakhala m'Gileadi m'Basana, ndi m'midzi yace, ndi podyetsa pace ponse pa Saroni, mpaka malire ao.

17. Onsewo anawerengedwa monga mwa mabuku a cibadwidwe cao, masiku a Yotamu mfumu ya Yuda, ndi m'masiku a Yerobiamu mfumu ya Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 5