Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 29:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mfumu Davide ananenanso kwa khamu lonse, Mulungu wasankha mwana wanga Solomo yekha, ndiye mnyamata ndi wosakhwima; ndipo nchitoyi ndi yaikuru, pakuti cinyumbaci siciri ca munthu, koma ca Yehova Mulungu.

2. Ndi mphamvu yanga yonse tsono ndakonzeratu nyumba ya Mulungu wanga, golidi wa zija zagolidi ndi siliva wa zija zasiliva, ndi mkuwa wa zija zamkuwa, citsulo ca zija zacitsulo, ndi mtengo wa zija zamtengo, miyala yaberulo, ndi miyala yoikika, miyala yokometsera, ndi ya mawanga mawanga, ndi miyala ya mtengo wace ya mitundu mitundu ndi miyala yansangalabwe yocuruka.

3. Ndiponso popeza ndikondwera nayo nyumba ya Mulungu wanga, cuma cangacanga ca golidi ndi siliva ndiri naco ndicipereka ku nyumba ya Mulungu wanga, moenjezera ndi zonse ndazikonzeratu nyumba yopatulikayo;

4. ndico matalente zikwi zitatu za golidi, golidi wa Ofiri; ndi matalente zikwi zisanu ndi ziwiri a siliva woyengetsa, kumamatiza nazo makoma a nyumbazi;

5. golidi wa zija zagolidi, ndi siliva wa zija zasiliva, ndi za nchito ziri zonse akuzipanga manja a amisiri. Ndani uyo afuna mwini kudzipatulira kwa Yehova lero line?

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 29