Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 27:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ana a Israyeli monga mwa ciwerengo cao, kunena za akuru a nyumba za makolo ao, ndi akazembe a zikwi, ndi a mazana, ndi akapitao ao akutumikira mfumu mu nchito iri yonse ya magawidwe, akulowa ndi kuturuka mwezi ndi mwezi, miyezi yonse ya caka, cigawo ciri conse nca amuna zikwi makumi awiri mphambu zinai.

2. Woyang'anira cigawo coyamba ca mwezi, woyamba ndiye Yasobeamu mwana wa Zabidiyeli; m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

3. Ndiye wa ana a Perezi, mkuru wa akazembe onse a khamu mwezi woyamba.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 27