Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 26:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. A Amirami, a Aizari, a Ahebroni, a Auziyeli;

24. ndi Sebueli mwana wa Gerisomu, mwana wa Mose, ndiye mkuru woyang'anira zuma.

25. Ndi abale ace a Eliezeri: Rehabiya mwana wace, ndi Yesava mwana wace ndi Yorramu mwana wace, ndi Zikiri mwana wace, ndi Selomoti mwana wace.

26. Selomoti amene ndi abale ace anayang'anira cuma conse ca zinthu zopatulika, zimene Davide mfumu ndi akuru a nyumba za akulu, akuru a zikwi ndi mazana, adazipatula.

27. Kutenga pa zofunkha kunkhondo, anapatulako kukonzera nyumba ya Yehova.

28. Ndipo zonse adazipatula Samueli mlauli, ndi Sauli mwana wa Kisi, ndi Abineri mwana wa Neri, ndi Yoabu mwana wa Zeruya; ali yense anapatula kanthu kali konse, anazisunga Selomoti ndi abale ace.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 26