Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 26:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Meselemiya anali ndi ana, woyamba Zekariya, waciwiri Yedyaeli, wacitatu Zebadiya, wacinai Yatiniyeli,

3. wacisanu Elamu, wacisanu ndi cimodzi Yohanana, wacisanu ndi ciwiri Elihunai.

4. Ndipo Obedi Edomu anali nao ana, woyamba Semaya, waciwiri Yozabadi, wacitatu Yowa, wacinai Sakara, wacisanu Netaneli,

5. wacisanu ndi cimodzi Amiyeli, wacisanu ndi ciwiri Isakara, wacisanu ndi citatu Peuletai; pakuti Mulungu adamdalitsa.

6. Kwa Semaya mwana wace yemwe kunabadwa ana, akulamulira nyumba ya atate wao; pakuti anali ngwazi zamphamvu.

7. Ana a Semaya: Otini, ndi Refaeli, ndi Obedi, Elzabadi, amene abale ao ndiwo odziwa mphamvu, Elihu, ndi Semakiya.

8. Onsewa ndiwo a ana a Obedi Edomu; iwo ndi ana ao, ndi abale ao, anthu odziwa mphamvu yakutumikira, makumi asanu ndi limodzi mphambu awiri a Obedi Edomu.

9. Ndi Meselemiya anali ndi ana, ndi abale odziwa mphamvu khumi mphambu asanu ndi atatu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 26