Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 26:15-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Obedi Edomu kumwela, ndi ana ace nyumba ya akatundu.

16. Supimu ndi Hosa kumadzulo, ku cipata ca Saleketi, ku mseu wokwerapo, udikiro pandunji pa udikiro.

17. Kum'mawa kunali Alevi asanu ndi mmodzi, kumpoto anai tsiku ndi tsiku, kumwela anai tsiku ndi tsiku, ndi a nyumba ya akatundu awiri ndi awiri.

18. Ku Parabara kumadzulo anai kumseu, ndi awiri ku Parabara.

19. Awa ndi magawidwe a odikira; a ana a Akora, ndi a ana a Merari.

20. Ndipo wa Alevi, Ahiya anayang'anira cuma ca nyumba ya Mulungu, ndi cuma ca zopatulika.

21. Ana a Ladani: ana a Ladani a Agerisoni, akuru a nyumba za makolo a Ladani Mgerisoni, Yehieli.

22. Ana a Yehieli: Zetamu ndi Yoeli mbale wace, oyang'anira cuma ca nyumba ya Yehova.

23. A Amirami, a Aizari, a Ahebroni, a Auziyeli;

24. ndi Sebueli mwana wa Gerisomu, mwana wa Mose, ndiye mkuru woyang'anira zuma.

25. Ndi abale ace a Eliezeri: Rehabiya mwana wace, ndi Yesava mwana wace ndi Yorramu mwana wace, ndi Zikiri mwana wace, ndi Selomoti mwana wace.

26. Selomoti amene ndi abale ace anayang'anira cuma conse ca zinthu zopatulika, zimene Davide mfumu ndi akuru a nyumba za akulu, akuru a zikwi ndi mazana, adazipatula.

27. Kutenga pa zofunkha kunkhondo, anapatulako kukonzera nyumba ya Yehova.

28. Ndipo zonse adazipatula Samueli mlauli, ndi Sauli mwana wa Kisi, ndi Abineri mwana wa Neri, ndi Yoabu mwana wa Zeruya; ali yense anapatula kanthu kali konse, anazisunga Selomoti ndi abale ace.

29. A Aizara: Kenaniya ndi ana ace anacita nchito ya pabwalo ya Israyeli, akapitao ndi oweruza mirandu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 26