Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 26:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. waciwiri Hilikiya, wacitatu Tebaliya, wacinai Zekariya; ana ndi abale onse a Hosa ndiwo khumi ndi atatu.

12. Mwa iwowa munali magawidwe a odikira, mwa akulu a amuna akucita udikiro wao, monga abale ao, kutumikira m'nyumba ya Yehova.

13. Ndipo anacita maere ang'ono ndi akuru, monga mwa nyumba za makolo ao, kucitira zipata zonse.

14. Ndi maere a kum'mawa anagwera Selemiya. Ndipo anacitira maere Zekariya mwana wace, phungu wanzeru, ndi maere anamgwera kumpoto;

15. Obedi Edomu kumwela, ndi ana ace nyumba ya akatundu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 26