11. waciwiri Hilikiya, wacitatu Tebaliya, wacinai Zekariya; ana ndi abale onse a Hosa ndiwo khumi ndi atatu.
12. Mwa iwowa munali magawidwe a odikira, mwa akulu a amuna akucita udikiro wao, monga abale ao, kutumikira m'nyumba ya Yehova.
13. Ndipo anacita maere ang'ono ndi akuru, monga mwa nyumba za makolo ao, kucitira zipata zonse.
14. Ndi maere a kum'mawa anagwera Selemiya. Ndipo anacitira maere Zekariya mwana wace, phungu wanzeru, ndi maere anamgwera kumpoto;
15. Obedi Edomu kumwela, ndi ana ace nyumba ya akatundu.